Zephaniah 2:15 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Umenewo ndiwo mzinda umene unkadzimva kuti ndi wokhazikika, umene mumtima mwake unkati, “Ine pano! Palibenso wina ai!” Tauwonani m'mene wasakazikira tsopano! Wasanduka bwinja lokhalamo nyama zakuthengo. Aliyense wodutsamo azidzangotsonya nkumapukusa mutu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Uwu ndi mudzi wosekererawo unakhala wosasamalira, unanena m'mtima mwake, Ine ndine, ndi wopanda ine palibe wina; ha! Wasanduka bwinja, mogonera nyama za kuthengo! Yense wakuupitirira adzatsonya mtsonyo, ndi kupukusa mutu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Umenewu ndiye mzinda wosasamala umene kale unali wotetezedwa. Unkanena kuti mu mtima mwake, “Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.” Taonani lero wasanduka bwinja, kokhala nyama zakutchire! Onse owudutsa akuwunyoza ndi kupukusa mitu yawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Uwu ndi mudzi wosekererawo unakhala wosasamalira, unanena m'mtima mwace, Ine ndine, ndi wopanda ine palibe wina; ha! wasanduka bwinja, mogonera nyama za kuthengo! yense wakuupitirira adzatsonya mtsonyo, ndi kupukusa mutu.