Zephaniah 2:7 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kumeneko kudzakhala dziko la otsala a m'banja la Yuda. Azidzadyetsa nkhosa zao m'mbali mwanyanjamo, ndipo madzulo azidzagona ku nyumba za ku Asikeloni. Pakuti Chauta, Mulungu wao adzaŵasamalira, ndiye amene adzaŵabwezere ufulu wao.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo dziko la kunyanja lidzakhala la otsala a nyumba ya Yuda; adzadyetsa zoweta zao pamenepo; madzulo adzagona m'nyumba za Asikeloni; pakuti Yehova Mulungu wao adzawazonda, nadzabweza undende wao.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda; adzapezako msipu. Nthawi ya madzulo adzagona mʼnyumba za Asikeloni. Yehova Mulungu wawo adzawasamalira; adzabwezeretsa mtendere wawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo dziko la kunyanja lidzakhala la otsala a nyumba ya Yuda; adzadyetsa zoweta zao pamenepo; madzulo adzagona m'nyumba za Asikeloni; pakuti Yehova Mulungu wao adzawazonda, nadzabweza undende wao.