bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
2 Samuel 22
2 Samuel 22
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 21
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 23 →
1
Ndipo Davide analankhula kwa Yehova mau a nyimbo iyi tsikuli Yehova anampulumutsa m'dzanja la adani ake onse, ndi m'dzanja la Saulo.
2
Ndipo anati, Yehova ndiye thanthwe langa, ndi ngaka yanga, ndi Mpulumutsi wanga, wangadi.
3
Mulungu wa thanthwe langa, Iye ndidzamkhulupirira; chikopa changa, ndi nyanga ya chipulumutso changa, nsanja yanga yaitali, ndi populumukirapo panga; Mpulumutsi wanga, mundipulumutsa kuchiwawa.
4
Ndidzaitana kwa Yehova amene ayenera timtamande; chomwecho ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.
5
Pakuti mafunde a imfa anandizinga, mitsinje ya zopanda pake inandiopsa ine.
6
Zingwe za kumanda zinandizingira; misampha ya imfa inandifikira ine.
7
M'kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova, inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga; ndipo Iye anamva mau anga ali m'Kachisi wake, ndi kulira kwanga kunafika ku makutu ake.
8
Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira. Maziko a dziko la kumwamba anasunthika. Nagwedezeka, chifukwa Iye anakwiya.
9
M'mphuno mwake munatuluka utsi, ndi moto wotuluka m'kamwa mwake unaononga; makala anayaka nao.
10
Anaweramitsa miyambanso, natsika; ndipo mdima wandiweyani unali pansi pa mapazi ake.
11
Ndipo Iye anaberekeka pa kerubi nauluka; inde anaoneka pa mapiko a mphepo.
12
Ndipo anayesa mdimawo ngati mahema omzungulira Iye, kusonkhana kwa madzi ndi mitambo yochindikira ya mlengalenga.
13
Cheza cha pamaso pake makala a moto anayaka.
14
Yehova anagunda kumwamba; ndipo Wam'mwambamwamba ananena mau ake.
15
Ndipo Iye anatumiza mivi, nawawaza; mphezi, nawaopsa.
16
Pamenepo m'munsi mwa nyanja munaoneka, maziko a dziko anaonekera poyera, ndi mtonzo wa Yehova, ndi mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwake.
17
Iye anatumiza kuchokera kumwamba nanditenga; Iye ananditulutsa m'madzi aakulu.
18
Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu.
19
Anandifikira ine tsiku la tsoka langa; koma Yehova anali mchirikizo wanga.
20
Iye ananditulutsanso ku malo akulu; Iye anandipulumutsa, chifukwa akondwera ndi ine.
21
Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa; monga mwa kuyera kwa manja anga anandipatsa mphotho.
22
Pakuti ndinasunga njira za Yehova, osapatukira ku zoipa kusiya Mulungu wanga.
23
Pakuti maweruzo ake onse anali pamaso panga; ndipo za malemba ake, sindinawapatukira.
24
Ndinakhalanso wangwiro kwa Iye, ndipo ndinadzisunga kusachita kuipa kwanga.
25
Chifukwa chake Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa; monga mwa kuyera kwanga pamaso pake.
26
Ndi chifundo Inu mudzadzionetsa wachifundo, ndi munthu wangwiro mudzadzionetsa wangwiro.
27
Ndi oyera mtima mudzadzionetsa woyera mtima; ndi otsutsatsutsa mudzadzionetsa wopotoza.
28
Ndipo mudzapulumutsa anthu osautsidwa; koma maso anu ali pa odzikuza kuti muwachepetse.
29
Pakuti Inu ndinu nyali yanga, Yehova; ndipo Yehova adzaunika mumdima mwanga.
30
Pakuti ndi Inu ndithamangira gulu; ndi Mulungu wanga ndilumphira linga.
31
Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro; mau a Yehova anayesedwa; Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye.
32
Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova? Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu?
33
Mulungu ndiye linga langa lamphamvu; ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.
34
Iye asandutsa mapazi ake akunga mapazi a mbawala; nandiika pa misanje yanga.
35
Iye aphunzitsa manja anga nkhondo; kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa.
36
Ndiponso munandipatsa chikopa cha chipulumutso chanu; ndi kufatsa kwanu kunandikulitsa.
37
Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga, ndi mapazi anga sanaterereke.
38
Ndinapirikitsa adani anga, ndi kuwaononga; ndiponso sindinabwerera mpaka nditawatha.
39
Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sakhoza kuuka, inde anagwa pansi pa mapazi anga.
40
Pakuti Inu munandimanga m'chuuno ndi mphamvu ya kunkhondo; munandigonjetsera akundiukira.
41
Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo, kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.
42
Anayang'ana iwo, koma panalibe wopulumutsa; ngakhale kwa Yehova, koma Iye sanawayankhe.
43
Pomwepo ndinawasansantha asalale ngati fumbi la padziko, ndinawapondereza ngati dothi la m'makwalala.
44
Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga; munandisunga ndikhale mutu wa amitundu; Anthu amene sindinawadziwa adzanditumikira ine.
45
Alendo adzandigonjera ine, pakumva za ine, adzandimvera pomwepo.
46
Alendo adzafota, nadzabwera ndi kunthunthumira otuluka mokwiririka mwao.
47
Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa; ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la chipulumutso changa;
48
inde Mulungu wakundibwezera chilango ine, ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.
49
Amene anditulutsa kwa adani anga; inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira; mundipulumutsa kwa munthu wachiwawa.
50
Chifukwa chake ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu, ndipo ndidzaimba zolemekeza dzina lanu.
51
Iye apatsa mfumu yake chipulumutso chachikulu; naonetsera chifundo wodzozedwa wake, kwa Davide ndi mbeu yake ku nthawi zonse.
← Chapter 21
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 23 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24