bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Mark 2
Mark 2
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 1
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 3 →
1
Patapita masiku pang'ono, Yesu adabwereranso ku Kapernao, anthu nkumva kuti ali kunyumba kwao.
2
Anthu ochuluka adasonkhana m'nyumbamo, kotero kuti munalibenso malo ngakhale pakhomo pomwe. Iye ankaŵalalikira mau a Mulungu.
3
Anthu ena anai adaanyamula munthu wa ziwalo zakufa, kubwera naye kwa Yesu.
4
Koma sadathe kufika naye pafupi ndi Yesuyo chifukwa cha kuchuluka kwa anthu. Choncho adakwera pa denga, nangosasula dengalo kuyang'anana ndi pamene Yesu analiri, nkutsitsira pachiboopo machira amene adaanyamulira munthu uja.
5
Poona chikhulupiriro chaocho, Yesu adauza munthu wa ziwalo zakufayo kuti, “Mwana wanga, machimo ako akhululukidwa.”
6
Koma pamenepo panalinso aphunzitsi ena a Malamulo a Mose. Iwowo adayamba kudzifunsa mumtima mwao kuti,
7
“Kodi Iyeyu angalankhule bwanji motere? Si kunyoza Mulungu kumeneku? Ndani angakhululukire machimo, si Mulungu yekha kodi?”
8
Koma Yesu adaadziŵa kuti akuganiza zimenezi mumtima mwao, motero adaŵafunsa kuti, “Bwanji mukuganiza zimenezo mumtima mwanu?
9
Chapafupi koposa nchiti, kumuuza wa ziwalo zakufayu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Dzuka, nyamula machira ako, yamba kuyenda?’
10
Koma kuti mudziŵe kuti Mwana wa Munthu ali nazo mphamvu pansi pano zokhululukira machimo, onani.” Pamenepo adauza wofa ziwalo uja kuti,
11
“Iwe, dzuka, tenga machira ako, uzipita kumudzi.”
12
Munthu uja adadzukadi, natenga machira ake aja nkutuluka, onse aja akuwona. Anthu onse aja adazizwa kwambiri, nayamba kutamanda Mulungu nkumanena kuti, “Zoterezi ife sitinaziwone nkale lonse.”
13
Yesu adapitanso ku nyanja. Anthu ambirimbiri adafika komweko, ndipo Iye adayamba kuŵaphunzitsa.
14
Pamene Yesu ankayenda, adaona Levi, mwana wa Alifeyo, ali pa ntchito m'nyumba ya msonkho. Adamuuza kuti, “Iwe, unditsate.” Iye adanyamuka nkumamutsatadi.
15
Tsono pamene Yesu ankadya m'nyumba mwa Leviyo, panali anthu ambiri okhometsa msonkho ndi anthu ochimwa, odzadya nao ndi Yesuyo ndi ophunzira ake. Anali anthu ambiri ndithu amene adaatsagana naye.
16
Pamene aphunzitsi a Malamulo a m'gulu la Afarisi adaona kuti Yesu akudya ndi anthu ochimwa, ndiponso ndi anthu okhometsa msonkho, adafunsa ophunzira ake kuti, “Bwanji akudya pamodzi ndi okhometsa msonkho ndiponso ndi anthu ochimwa?”
17
Yesu atamva zimenezo adaŵayankha kuti, “Anthu amene ali bwino sasoŵa sing'anga ai, koma amene akudwala. Inetu sindidabwere kudzaitana anthu olungama, koma anthu ochimwa.”
18
Nthaŵi ina ophunzira a Yohane Mbatizi ndiponso Afarisi ankasala zakudya. Anthu adadza kwa Yesu namufunsa kuti, “Kodi bwanji ophunzira a Yohane ndi ophunzira a Afarisi amasala zakudya, koma ophunzira anu ai?”
19
Yesu adati, “Kani anzake a mkwati angathe kumasala zakudya pamene mkwati ali nao pomwepo? Chosatheka! Pamene mkwati ali nao pomwepo iwo sangamasale zakudya.
20
Koma idzafika nthaŵi pamene adzaŵachotsere mkwatiyo. Pamenepo ndiye azidzasala zakudya.
21
“Munthu satenga chigamba cha nsalu yatsopano nkuchisokerera pa chovala chakale. Chifukwa akatero, chigamba chatsopano chija chimakoka nkunyotsolako chovala chakalecho, ndiye kung'ambika kwake kumakhala kwakukulu koposa kale.
22
Ndiponso munthu sathira vinyo watsopano m'matumba achikopa akale. Chifukwa akatero, vinyoyo amaphulitsa matumba aja, ndipo choncho vinyo uja amatayika, matumbawo nkutha ntchito. Koma vinyo watsopano amamuthira m'matumba atsopanonso.”
23
Pa tsiku lina la Sabata Yesu ankadutsa m'minda ya tirigu. Akuyenda choncho, ophunzira ake adayamba kuthyolako ngala za tirigu nkumadya.
24
Apo Afarisi adafunsa Yesu kuti, “Bwanji ophunzira anuŵa akuchita zimene siziloledwa pa tsiku la Sabata?”
25
Iye adati, “Bwanji mukuchita ngati simudaŵerenge konse zimene adaachita Davide, pamene iye ndi anzake adaazingwa nayo njala?
26
Suja adaaloŵa m'nyumba ya Mulungu, pa nthaŵi imene Abiyatara anali mkulu wa ansembe onse, nkukadya buledi woperekedwa kwa Mulungu? Chonsecho buledi ameneyo nkosaloledwa kuti wina aliyense nkumudya, kupatula ansembe okha. Komanso adaagaŵirako anzake aja amene adaali naye.”
27
Tsono Yesu popitiriza mau, adauza Afarisiwo kuti, “Mulungu adaika tsiku la Sabata kuti likhale lothandiza anthu. Sadalenge anthu kuti akhale akapolo a tsiku la Sabata ai.
28
Choncho Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro wonse pa zokhudza tsiku la Sabata.”
← Chapter 1
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 3 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16