bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
1 Samuel 18
1 Samuel 18
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 17
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 19 →
1
Davide atatha kulankhula ndi Saulo, mtima wa Yonatani udagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo Yonatani adakonda Davideyo monga momwe ankadzikondera iye mwini.
2
Mwakuti adamtenga Davideyo tsiku lomwelo, osamlola kuti abwerere ku banja kwa bambo wake.
3
Adachita naye chipangano chifukwa ankamkonda monga momwe ankadzikondera iye mwini.
4
Tsono adavula mwinjiro umene anali nawo napatsa Davide pamodzi ndi zovala zankhondo, lupanga lake, uta wake ndi lamba wake.
5
Tsono kulikonse kumene Davide ankatumidwa ndi Saulo kuti akamenye nkhondo, ankapambana adani. Motero Saulo adamuika Davide kuti akhale mtsogoleri wa ankhondo. Chimenechi chidakondwetsa anthu onse, ngakhalenso atsogoleri a ankhondo a Saulo.
6
Pamene anthu ankabwerera kwao, Davide atapha Mfilisti uja, akazi adatuluka m'mizinda yonse ya Aisraele akuimba ndi kuvina, kuti achingamire mfumu Saulo. Ankaimba ndi kumavina mokondwa, kwinaku ng'oma ndi zitoliro zikugundika.
7
Akaziwo ankapolokezana akukondwerera namati, “Saulo wapha zikwi inde, koma Davide wapha zikwi khumikhumi!”
8
Apo Saulo adapsa mtima kwambiri, mau ameneŵa adaipidwa nawo. Adati, “Davide amuŵerengera zikwi zochuluka, koma ine andiŵerengera zikwi zochepa. Nanga chamkhaliranso nchiyani? Si ufumu basi?”
9
Motero Saulo ankamuwona ndi diso loipa Davide kuyambira tsiku limenelo.
10
M'maŵa mwake mzimu woipa uja udamtsikira Saulo, ndipo adayamba kubwebweta moyaluka m'nyumba mwake. Davide ankamuimbira zeze, monga momwe ankachitira tsiku ndi tsiku. Saulo anali ndi mkondo m'manja mwake.
11
Tsono adaponya mkondowo ndipo mumtima mwake adati, “Ndimubaya ndi kumkhomera ku chipupa.” Koma Davide adauleŵa. Zidachitika kaŵiri konse.
12
Pambuyo pake Saulo adayamba kuwopa Davide, chifukwa choti tsopano Chauta anali ndi Davide, kumsiya iyeyo.
13
Motero Saulo adamtuma Davide kwina kwake, ndipo adamuika kuti akhale mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Davide ankapita namabwera akuŵatsogolera.
14
Ndipo ankapambana pa zonse zimene ankachita, chifukwa Chauta anali naye.
15
Tsono pamene Saulo adaona kuti Davide akupambana kwambiri, adayamba kuchita naye mantha.
16
Koma anthu onse a ku Israele ndi a ku Yuda ankamkonda Davide, chifukwa iyeyu ankaŵatsogolera namapambana pa zonse.
17
Tsiku lina Saulo adauza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkulu. Ndidzakupatsa kuti akhale mkazi wako. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Chauta.” Potero Saulo ankaganiza kuti, “Ndisamuphe ndine ndi dzanja langa, koma amuphe ndi Afilisti.”
18
Tsono Davide adafunsa Saulo kuti, “Kodi ine ndine yani, ndipo abale anga ndi banja la bambo wanga ndife yani m'dziko la Israele, kuti ine nkukhala mkamwini wa mfumu?”
19
Koma pa nthaŵi yoti Merabi, mwana wa Saulo, akwatiwe ndi Davide, bambo wake adampereka kwa Adriyele Mmehola, kuti akhale mkazi wake.
20
Komabe Mikala, mwana wina wamkazi wa Saulo, ankakonda Davide. Saulo atamva, adakondwa kwambiri.
21
Adaganiza kuti, “Ndimpatse amkwatire, kuti adzakhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo Afilisti adzamupha.” Nchifukwa chake Saulo adauza Davide kachiŵiri kuti, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
22
Motero adalamula nduna zake kuti, “Mulankhule naye Davide pambali nkumuuza kuti, ‘Mfumu imakukonda, ndipo ngakhale nduna zake zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’ ”
23
Nduna za Saulo zidamuuza Davide mau amenewo. Koma iye adati, “Kani mukuchiyesa chinthu chapafupi kukhala mkamwini wa mfumu? Kodi simukuwona kuti ndine wosauka ndi wosatchuka?”
24
Nduna za Saulo zidamuuza zonse zimene Davide adaanena.
25
Tsono Saulo adati, “Kamuuzeni kuti, sindikufuna chiwongo cha mtundu uliwonse ai, ndingofuna timakungu ta nsonga za mavalo a Afilisti 100, kuti ndilipsire adani anga.” Potero Saulo ankaganiza zoti Davide aphedwe ndi Afilisti.
26
Ndiye nduna za Saulozo zitamuuza Davide mau ameneŵa, zidamkondweretsa kuti akhale mkamwini wa mfumu. Nthaŵi yoti atenge mkazi wake isanakwane,
27
Davide adanyamuka napita pamodzi ndi ankhondo ake, ndipo adakapha Afilisti 200. Adabwera nato timakungu tija natipereka kwa mfumu, kuti choncho akhale mkamwini wake. Apo Saulo adapatsa Davideyo mwana wake Mikala, kuti akhale mkazi wake.
28
Koma Saulo atazindikira kuti Chauta ali naye Davide, ndiponso kuti mwana wake Mikala ankamkonda Davideyo,
29
adamuwopabe kwambiri ndi kudana naye moyo wake wonse.
30
Tsono pamene Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, nthaŵi zonse Davide ankapambana kwambiri kuposa atsogoleri ena onse a ankhondo a Saulo. Choncho dzina lake la Davide lidatchuka kwambiri.
← Chapter 17
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 19 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31