bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
/
Proverbs 6
Proverbs 6
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
← Chapter 5
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 7 →
1
Mwananga, ngati waperekera mnzako cikole, Ngati wapangana kulipirira mlendo,
2
Wakodwa ndi mau a m'kamwa mwako, Wagwidwa ndi mau a m'kamwa mwako.
3
Cita ici tsono; mwananga, nudzipulumutse; Popeza walowa m'dzanja la mnzako, Pita nudzicepetse, numdandaulire mnzako,
4
Usaone tulo m'maso mwako, Ngakhale kuodzera zikope zako.
5
Dzipulumutse wekha ngati mphoyo ku dzanja la msaki, Ndi mbalame ku dzanja la msodzi.
6
Pita kunyerere, wolesi iwe, Penya njira zao nucenjere;
7
Ziribe mfumu, Ngakhale kapitao, ngakhale mkuru;
8
Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe; Nizituta dzinthu zao m'masika.
9
Udzagona mpaka liti, wolesi iwe? Udzauka ku tulo tako liti?
10
Tulo ta pang'ono, kuodzera pang'ono, Kungomanga manja pang'ono, ndi kugona;
11
Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala, Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.
12
Munthu wopanda pace, mwamuna wamphulupulu; Amayenda ndi m'kamwa mokhota;
13
Amatsinzinira ndi maso ace, napalasira ndi mapazi ace, Amalankhula ndi zala zace;
14
Zopotoka ziri m'mtima mwace, amaganizira zoipa osaleka; Amapikisanitsa anthu.
15
Cifukwa cace tsoka lace lidzadza modzidzimuka; Adzasweka msanga msanga, palibe compulumutsa.
16
Ziripo zinthu zisanu ndi cimodzi Mulungu azida; Ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:
17
Maso akunyada, lilime lonama, Ndi manja akupha anthu osacimwa;
18
Mtima woganizira ziwembu zoipa, Mapazi akuthamangira mphulupulu mmangu mmangu;
19
Mboni yonama yonong'ona mabodza, Ndi wopikisanitsa abale.
20
Mwananga, sunga malangizo a atate wako, Usasiye malamulo a mako;
21
Uwamange pamtima pako osaleka; Uwalunze pakhosi pako.
22
Adzakutsogolera ulikuyenda, Ndi kukudikira uli m'tulo, Ndi kulankhula nawe utauka.
23
Pakuti malangizo ndi nyali, malamulo ndi kuunika; Ndi zidzudzulo za mwambo ndizo njira ya moyo;
24
Zikucinjiriza kwa mkazi woipa, Ndi ku lilime losyasyalika la mkazi waciwerewere.
25
Asakucititse kaso m'mtima mwako, Asakukole ndi zikope zace.
26
Pakuti ukayamba ndi mkazi wadama, udzamariza ndi nyenyeswa; Ndipo mkazi wa mwini amasaka moyo wa mtengo wapatari.
27
Kodi mwamuna angatenge moto pa cifuwa cace, Osatentha zobvala zace?
28
Pena kodi mwamuna angayende pa makala oyaka, Osapsya mapazi ace?
29
Comweco wolowa kwa mkazi wa mnzace; Womkhudzayo sadzapulumuka cilango.
30
Anthu sanyoza mbala ikaba, Kuti ikhutitse mtima wace pomva njala;
31
Koma ikapezedwa idzabwezera kasanu ndi kawiri; Idzapereka cuma conse ca m'nyumba yace.
32
Wocita cigololo ndi mkazi alibe nzeru; Wofuna kuononga moyo wace wace ndiye amatero.
33
Adzalasidwa nanyozedwa; Citonzo cace sicidzafafanizidwa.
34
Pakuti nsanje ndiyo ukali wa mwamuna, Ndipo sadzacitira cifundo tsiku lobwezera cilango.
35
Sadzalabadira ciombolo ciri conse, Sadzapembedzeka ngakhale ucurukitsa malipo,
← Chapter 5
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 7 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31