bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Deuteronomy 16
Deuteronomy 16
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 15
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 17 →
1
Muzilemekeza Chauta, Mulungu wanu, pakuchita chikondwerero cha Paska pa mwezi wa Abibu. Chifukwa usiku wina mwezi umenewu, mpamene Chauta adakutulutsani ku Ejipito.
2
Muzipereka nsembe za chikondwerero cha Paska kwa Chauta, Mulungu wanu. Muphe nkhosa kapena ng'ombe pa malo amene Chauta adzasankhule kuti anthu azidzapembedzerapo.
3
Nyama ya nsembeyo musadye ndi buledi wotupitsa. Pa masiku asanu ndi aŵiri, muzidya nyamayo ndi buledi wosatupitsa ndiye kuti buledi wamazunzo, pakuti mudatuluka ku Ejipito mothaŵa. Motero masiku onse a moyo wanu, mudzakumbukira tsiku limene mudatuluka ku Ejipito.
4
Pa masiku asanu ndi aŵiri munthu wina aliyense asadzasunge chofufumitsira buledi m'nyumba mwake m'dziko mwanumo. Nyama imene idaphedwa madzulo pa tsiku loyamba, muzidzaidya kusanache.
5
Musapereke nsembe ya Paska kulikonse ku dziko limene Chauta, Mulungu wanu, akukupatsani.
6
Muziphera pa malo amodzi opembedzerapo aja. Muzichita zimenezi poloŵa dzuŵa, ndiye kuti nthaŵi yomwe ija imene mudachoka ku Ejipito.
7
Muziphika nyamayo ndi kuidyera pa malo achipembedzo amodziwo, ndipo muzibwerera ku zithando zanu m'maŵa mwake.
8
Masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wosatupitsa. Koma pa tsiku lachisanu ndi chiŵiri, muzisonkhana kuti mupembedze Chauta, Mulungu wanu, ndipo musadzagwire ntchito pa tsiku limenelo.
9
Muŵerenge masabata asanu ndi aŵiri kuyambira nthaŵi imene mwayamba kudula tirigu.
10
Tsono muchite chikondwerero cha kholola, cholemekeza Chauta, Mulungu wanu, pakumpatsa chopereka chaufulu, molingana ndi madalitso amene Iye wakupatsani.
11
Mukhale okondwa pamaso pa Chauta, Mulungu wanu, inuyo pamodzi ndi mwana wanu wamwamuna, mwana wanu wamkazi, mtumiki wamu wamwamuna, mdzakazi wanu, Alevi amene ali m'mizinda mwanu, alendo, ana amasiye ndi akazi amasiye, amene amakhala nanu pamodzi m'mizinda mwanu. Zimenezi muzichitira pa malo opembedzerapo aja.
12
Kumbukirani kuti mudaali akapolo ku Ejipito. Motero malamulo ameneŵa muziŵasungadi mosamala.
13
Mutatuta tirigu wanu yense, ndiponso mutafinya mphesa zanu, muzidzachita chikondwerero cha misasa masiku asanu ndi aŵiri.
14
Musangalale pa chikondwererocho, inuyo pamodzi ndi mwana wanu wamwamuna, mwana wanu wamkazi, mtumiki wanu wamwamuna, mdzakazi wanu, Alevi amene ali m'mizinda mwanu, alendo, ana amasiye ndi akazi amasiye, amene amakhala nanu m'mizinda mwanu.
15
Muzidzatamanda Chauta, Mulungu wanu, pochita chikondwerero chimenechi masiku asanu ndi aŵiri, pa malo amene Iye adzasankhule, chifukwa chakuti Chauta, Mulungu wanu, adzakhala atadalitsa kholola lanu ndi ntchito zanu zonse, kuti chimwemwe chanu chikhale chodzaza ndithu.
16
Anthu aamuna onse a mtundu wanu azidzabwera kudzapembedza Chauta, Mulungu wanu, ku malo achipembedzo, katatu pa chaka. Azidzafika pa nthaŵi ya Paska, pa nthaŵi ya chikondwerero cha kholola ndiponso pa nthaŵi ya chikondwerero cha misasa.
17
Ndipo pobwera pamaso pa Chauta, asamadzakhale chimanjamanja, koma munthu aliyense azidzabwera ndi mphatso monga momwe angathere, molingana ndi madalitso amene Chauta, Mulungu wanu, adampatsa.
18
M'fuko lililonse mudzasankhe anthu oweruza ndiponso akuluakulu ena mu mzinda uliwonse umene Chauta, Mulungu wanu, adzakupatseni. Anthu ameneŵa azidzaweruza anzao mosakondera.
19
Asadzachite zinthu mopanda chilungamo kapena kuweruza milandu mokondera. Asadzalandire chiphuphu, chifukwa ziphuphu zimadetsa m'maso ngakhale anthu anzeru ndipo zimalakwitsa anthu olungama poweruza.
20
Mukonde osati china ai, koma chilungamo chokha basi, kuti mudzalandiredi dziko limene Chauta, Mulungu wanu, akukupatsani ngati choloŵa chanu, ndi kukhazikikamo.
21
Musadzazike mtengo uliwonse wachipembedzo pambali pa guwa la Chauta, Mulungu wanu, limene mudzamange.
22
Ndipo musadzaimiritse miyala yachipembedzo, popeza kuti Chauta, Mulungu wanu, amadana nazo zimenezi.
← Chapter 15
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 17 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31
32
33
34