bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Proverbs 28
Proverbs 28
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 27
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 29 →
1
Woipa mtima amangodzithaŵira popanda wina wompirikitsa, koma wochita zabwino amalimba mtima ngati mkango.
2
Eni dziko akachita zaupandu, oŵalamulira amachuluka. Koma anthu akakhala omvetsa ndi odziŵa zinthu, dzikolo limakhazikika nthaŵi yaitali.
3
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake, ali ngati mvula yamkuntho yosasiya konse chakudya m'minda.
4
Amene samvera malamulo amatamanda anthu oipa mtima, koma otsata malamulo amatsutsana nawo.
5
Anthu oipa samvetsa kuti chilungamo nchiyani, koma amene amatsata kufuna kwa Chauta amachimvetsa kwathunthu.
6
Munthu wosauka amene amayenda mwaungwiro amaposa kwambiri munthu wolemera amene ali wonyenga.
7
Amene amatsata malamulo ndiye mwana wanzeru, koma amene amayenda ndi anthu adyera, amachititsa atate ake manyazi.
8
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja ndi pochikundika, chumacho amachikundikira ena amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9
Wina akamakana kumvera malamulo, ngakhale mapemphero ake amanyansira Mulungu.
10
Amene amasokeza anthu olungama kuti azitsata njira yoipa, adzagwa m'dzenje lake lomwe. Koma anthu amene alibe cholakwa adzalandira choloŵa chabwino.
11
Munthu wolemera amadziyesa wanzeru, koma munthu wosauka amene ali womvetsa zinthu, amamtulukira.
12
Anthu abwino akapambana, pamakhala chikondwerero chachikulu, koma oipa mtima akalandira ulamuliro, anthu amabisala.
13
Wobisa machimo ake sadzaona mwai, koma woulula ndi kuleka machimo, adzalandira chifundo.
14
Ndi wodala munthu amene amaopa Chauta nthaŵi zonse, koma woumitsa mtima wake adzagwa m'tsoka.
15
Monga muja umakhalira mkango wobangula kapena chimbalangondo cholusa, ndimonso imakhalira mfumu yoipa mtima kwa anthu osauka.
16
Wolamulira amene samvetsa zinthu amapondereza anthu mwankhanza, koma wodana ndi phindu loipa amatalikitsa masiku ake.
17
Munthu amene wapalamula mlandu wopha mnzake, akhale womathaŵathaŵa mpaka kufa kwake. Wina aliyense asamthandize.
18
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa, koma woyenda mokhotakhota adzagwa m'dzenje.
19
Wolima m'munda mwake adzakhala ndi chakudya chambiri, koma wonka nafuna zopanda pake adzasauka kwambiri.
20
Munthu wokhulupirika adzakhala ndi madalitso ambiri, koma wofunitsitsa kulemera msanga sadzalephera kupeza chilango.
21
Kuchita tsankho si kwabwino, komabe ena amaweruza mokondera chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22
Munthu wakaliwumira amafunitsitsa kulemera mofulumira, koma sadziŵa kuti umphaŵi udzamgwera.
23
Amene amadzudzula mnzake, potsiriza pake mnzakeyo adzamkonda kwambiri kupambana amene ali ndi mau oshashalika.
24
Wobera atate ake kapena amai ake namanena kuti kutero sikulakwa, ameneyo ndi mnzake wa munthu woononga.
25
Munthu waumbombo amautsa mkangano, koma wokhulupirira Chauta adzalemera.
26
Samvazaanzake nchitsiru, koma wotsata nzeru za ena adzapulumuka.
27
Amene amapatsa osauka sadzasoŵa kanthu koma amene amatsinzina dala kuti asaŵapenye, adzatembereredwa kwambiri.
28
Anthu oipa mtima akalandira ulamuliro, anthu amabisala, koma oipawo akaonongeka, anthu ochita chilungamo amapeza bwino.
← Chapter 27
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 29 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31