bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Proverbs 8
Proverbs 8
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 7
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 9 →
1
Kodi suja nzeru imaitana? Suja nzeru zomvetsera zinthu zimakweza mau ake?
2
Nzeru imakhala pa zitunda m'mbali mwa njira, imakaima pa mphambano za miseu.
3
Imafuula pafupi ndi zipata kumaso kwa mzinda, ndiponso pamakomo poloŵera, imati,
4
“Inu anthu, ndikukuitanani, kuitanaku ndikuitana anthu nonsenu.
5
Inu osadziŵa kanthunu, phunzirani nzeru, inu opusanu, khalani tcheru.
6
Mverani, ndikuuzani zazikulu kwambiri, pakamwa panga palankhula zolungama.
7
Pakamwa panga palankhula zoona, kulankhula zoipa nchinthu chonyansa m'kamwa mwanga.
8
Mau onse a pakamwa panga ngokondweretsa Mulungu, m'mau angawo mulibe zopotoka kapena zokhotakhota.
9
Mau anga ngoona kwa munthu womvetsa, ngokhoza kwa anthu odziŵa zinthu.
10
Landirani malangizo anga m'malo mwa siliva, funitsitsani kudziŵa zinthu, osati kuthamangira golide wabwino kwambiri.
11
Nzerutu ndi yabwino kuposa miyala yamtengowapatali. Zonse zimene ungazilakelake sizingafanefane ndi nzeru.
12
Ine nzeru ndimakhalira limodzi ndi kuchenjera. Ndimadziŵa zinthu ndipo ndimaganiza moyenera.
13
Kuwopa Chauta nkudana ndi zoipa. Kunyada, kudzitama, kuchita zoipa ndi kulankhula zonyenga, zonsezo ndimadana nazo.
14
Ndili ndi uphungu ndi maganizo abwino. Ndimamvetsa bwino zinthu, ndilinso ndi mphamvu.
15
Ndimathandiza mafumu polamulira ndine, olamulira ndimaŵathandiza ndine kulamula zolungama.
16
Ndine ndimathandiza akalonga polamula, ndine ndimathandiza akuluakulu poweruza m'dziko.
17
Anthu ondikonda, ine nzeru ndimaŵakonda, anthu ondifunafuna mosamala, amandipeza.
18
Ndili nacho chuma, ndili nawo ulemu, chuma chosatha ndiponso kukhuphuka konkirankira.
19
Zimene mumalandira kwa ine nzokoma kuposa golide, ngakhale golide wosalala. Phindu lochokera mwa ine nloposa siliva wabwino zedi.
20
Ndimachita zomwe zili zoyenera, sindipatuka kuchoka m'njira za chilungamo.
21
Ndimaŵapatsa chuma anthu ondikonda, ndi kudzaza nyumba zao zosungiramo chuma.
22
“Chauta adandilenga ine nzeru pa chiyambi cha ntchito zake. Mwa ntchito zake zakalekale woyambirira ndinali ine.
23
Ndidapangidwa masiku akalekale, pachiyambiyambi, dziko lapansi lisanalengedwe.
24
Nyanja zozama zisanalengedwe, padakalibe akasupe odzaza ndi madzi, nkuti ine nditabadwa kale.
25
Mapiri asanaumbidwe, magomo asanakhalepo, Mulungu anali atandilenga ineyo;
26
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake, lisanakhaleponso dothi loyamba la dziko lapansi.
27
Ine ndinalipo kale, pamene ankakhazikitsa zakumwamba, pamene ankalemba mzere wa malire a nyanja yozama,
28
pamene ankaika thambo m'malo mwake, pamene ankatsekula akasupe a m'nyanja yozama,
29
pamene ankaika malire a nyanja kuti madzi ake asabzole malirewo, pamene ankaika maziko a dziko lapansi.
30
Nthaŵiyo nkuti ndili pambalipa ngati mmisiri wake, ndikumkondweretsa tsiku ndi tsiku, ndikusangalala pamaso pake nthaŵi zonse.
31
Ndinkasangalala m'dziko lake lokhalamo anthu, ndi kumakondwa nawo ana a anthu.
32
“Ndipo tsopano, ana anga, tamverani, ngodala anthu amene amasunga malangizo anga.
33
Muzimva malangizo, kuti muzikhala anzeru, musamanyozere mau anga.
34
Ngwodala munthu amene amatchera khutu kwa ine, amene amakhala pakhomo panga tsiku ndi tsiku, amene amadikira pa chitseko changa.
35
Paja wondipeza ine, wapeza moyo, ndipo amapeza kuyanja pamaso pa Chauta.
36
Koma wosandipeza ine, akudzipweteka ameneyo. Onse odana ndi ine, ngokonda imfa amenewo.”
← Chapter 7
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 9 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31