bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Proverbs 4
Proverbs 4
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 3
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 5 →
1
Ana inu, mverani malangizo a atate anu, tcherani khutu, kuti mupate nzeru zodziŵira zinthu.
2
Ine ndikukupatsani malamulo abwino, musasiye zimene ndikukuphunzitsani.
3
Pamene ndinali mwana m'nyumba mwa atate anga, m'menemo ndili kamwana kapamtima ka amai anga,
4
atatewo adandiphunzitsa ndi mau akuti, “Ugwiritse mumtima mwako zimene ndikukuuzazi, usunge malamulo anga, kuti ukhale ndi moyo.
5
Usaiŵale mau a pakamwa pangaŵa, usatayane nawo, Ukhale ndi nzeru, ndiponso khalidwe la kumvetsa zinthu.
6
Usaisiye nzeru, ndipo idzakusunga. Uziikonda, ndipo idzakuteteza.
7
Chachikulu pa nzeru ndi ichi: Kaya nchiyani chimene ungapate, peza nzeruyo, usalephere kupata khalidwe la kumvetsa zinthu.
8
Uziilemekeza nzeruyo, ndipo idzakukweza. Uifungate ndipo idzakupatsa ulemerero.
9
Idzaika pamutu pako nsangamutu yokongola yamaluŵa. Idzakuveka chisoti chaufumu chaulemu.”
10
Mwana wanga, umvere ndi kuvomera zimene ndikunena. Ukatero, zaka za moyo wako zidzachuluka.
11
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera pa njira za moyo wolungama.
12
Ukamayenda, mapazi ako sazidzaombana. Ukamathamanga, sudzakhumudwa ai.
13
Uŵasamale zedi, pakuti moyo wako wagona pamenepo.
14
Usayende m'njira za anthu oipa, usatsate m'mapazi mwa anthu ochimwa.
15
Njira zao uzipewe, usapitemo konse. Uzilambalale, ndi kungozipitirira.
16
Iwo ajatu sangagone, mpaka atachita ndithu choipa. Tulo sangatiwone, mpaka atakhumudwitsapo munthu.
17
Paja kuchita zoipa ndiye chakudya chao, kuchita ndeu ndiye chakumwa chao.
18
Koma njira ya anthu okondweretsa Mulungu, ili ngati kuŵala kwa mbandakucha, kumene kumanka kukukulirakulira mpaka dzuŵa litafika pamutu.
19
Njira ya anthu oipa ili ngati mdima wandiweyani. Satha kuzindikira kuti aphunthwa pa chiyani.
20
Mwana wanga, mvetsetsa mau anga. Tchera khutu ku zimene ndikunena.
21
Zisachoke m'mutu mwakomu, uzisunge bwino mumtima mwako.
22
Paja zimampatsa moyo amene wazipeza, zimachiritsa thupi lake lonse.
23
Mtima wako uziwulonda bwino, pakuti m'menemo ndimo muli magwero a moyo.
24
Ulekeretu kulankhula zokhotakhota, usiyiretu kukamba zopotoka.
25
Maso ako aziyang'ana kutsogolo molunjika, uzipenya kutsogolo osacheukacheuka.
26
Uzisamala m'mene mukupita mapazi ako, ndipo njira zako zonse zidzakhala zosapeneketsa.
27
Usapatukire kumanja kapena kumanzere, usayende pamene pali choipa chilichonse.
← Chapter 3
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 5 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31