bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 1
Proverbs 1
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 2 →
1
Miyambo ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israele.
2
Kudziwa nzeru ndi mwambo; kuzindikira mau ozindikiritsa;
3
kulandira mwambo wakusamalira machitidwe, chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika;
4
kuchenjeza achibwana, kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;
5
kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira; ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;
6
kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lake, mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.
7
Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.
8
Mwananga, tamva mwambo wa atate wako, ndi kusasiya chilangizo cha amai ako;
9
pakuti izi ndi korona wa chisomo pamtu pako, ndi mkanda pakhosi pako.
10
Mwananga, akakukopa ochimwa usalole.
11
Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi, tilalire osachimwa opanda chifukwa;
12
tiwameze ali ndi moyo ngati manda, ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;
13
tidzapeza chuma chonse cha mtengo wake, tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;
14
udzachita nafe maere, tonse tidzakhala ndi chotengeramo chimodzi.
15
Mwananga, usayende nao m'njira; letsa phazi lako ku mayendedwe ao;
16
pakuti mapazi ao athamangira zoipa, afulumira kukhetsa mwazi.
17
Pakuti kutchera msampha pamaso pa mbalame ndi chabe;
18
ndipo awa abisalira mwazi waowao, alalira miyoyo yaoyao.
19
Mayendedwe a yense wopindula chuma monyenga ngotere; chilanda moyo wa eni ake.
20
Nzeru ifuula panja; imveketsa mau ake pabwalo;
21
iitana posonkhana anthu polowera pachipata; m'mudzi inena mau ake,
22
Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu? Onyoza ndi kukonda kunyoza, opusa ndi kuda nzeru?
23
Tembenukani pamene ndikudzudzulani; taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga, ndikudziwitsani mau anga.
24
Chifukwa ndaitana, ndipo munakana; ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;
25
koma munapeputsa uphungu wanga wonse, ndi kukana kudzudzula kwanga.
26
Inetu ndidzachitira chiphwete tsoka lanu, ndidzatonyola pakudza mantha anu;
27
pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula, ndi pofika tsoka lanu ngati kamvulumvulu; pakudza kwa inu vuto ndi nsautso.
28
Pamenepo adzandiitana, koma sindidzavomera; adzandifunatu, osandipeza ai;
29
chifukwa anada nzeru, sanafune kuopa Yehova;
30
anakana uphungu wanga, nanyoza kudzudzula kwanga konse;
31
momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao, nadzakhuta zolingalira zao.
32
Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa achibwana kudzawapha; ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.
33
Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka, nadzakhala phee osaopa zoipa.
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 2 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31