bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 28
Proverbs 28
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 27
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 29 →
1
Woipa athawa palibe momthamangitsa; koma olungama alimba mtima ngati mkango.
2
Pochimwa dziko akalonga ake achuluka; koma anthu ozindikira ndi odziwa alikhazikikitsa nthawi yaikulu.
3
Munthu waumphawi wotsendereza osauka akunga mvula yamadzi yokokolola dzinthu.
4
Omwe asiya chilamulo atama oipa; koma omwe asunga chilamulo akangana nao.
5
Oipa samvetsetsa chiweruzo; koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.
6
Waumphawi woyenda mwangwiro apambana ndi yemwe akhotetsa njira zake, angakhale alemera.
7
Wosunga chilamulo ndiye mwana wozindikira; koma mnzao wa adyera achititsa atate wake manyazi.
8
Wochulukitsa chuma chake, pokongoletsa ndi phindu, angokundikira yemwe achitira osauka chisoni.
9
Wopewetsa khutu lake kuti asamve chilamulo, ngakhale pemphero lake linyansa.
10
Wosocheretsa oongoka mtima alowe m'njira yoipa, adzagwa mwini m'dzenje lake; koma angwiro adzalandira cholowa chabwino.
11
Wolemera adziyesa wanzeru; koma wosauka wozindikira aululitsa zake.
12
Posekera olungama pali ulemerero wambiri; koma pouka oipa anthu amabisala.
13
Wobisa machimo ake sadzaona mwai; koma wakuwavomereza, nawasiya adzachitidwa chifundo.
14
Wodala munthu wakuopa kosalekeza; koma woumitsa mtima wake adzagwa m'zoipa.
15
Monga mkango wobangula ndi chilombo choyendayenda, momwemo mfumu yoipa ya anthu osauka.
16
Kalonga wosowa nzeru apambana kusautsa; koma yemwe ada chisiriro adzatanimphitsa moyo wake.
17
Wopalamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje; asamuletse.
18
Woyenda mwangwiro adzapulumuka; koma wokhota m'mayendedwe ake adzagwa posachedwa.
19
Wolima munda wake zakudya zidzamkwanira; koma wotsata anthu opanda pake umphawi udzamkwanira.
20
Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri; koma wokangaza kulemera sadzapulumuka chilango.
21
Chetera silili labwino, ngakhale kulakwa kuti ukadye kanthu.
22
Mwini diso lankhwenzule akangaza kulemera, osadziwa kuti umphawi udzamfikira.
23
Adzamkomera mtima wodzudzula m'tsogolo mwake, koposa wosyasyalika ndi lilime lake.
24
Wobera atate wake, pena amake, nati, Palibe kulakwa; ndiye mnzake wa munthu wopasula.
25
Wodukidwa mtima aputa makangano; koma wokhulupirira Yehova adzakula.
26
Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.
27
Wogawira aumphawi sadzasowa; koma wophimba maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28
Pouka oipa anthu amabisala; koma pakufa amenewo olungama achuluka.
← Chapter 27
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 29 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31