bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 2
Proverbs 2
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 1
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 3 →
1
Mwananga, ukalandira mau anga, ndi kusunga malamulo anga;
2
kutcherera makutu ako kunzeru, kulozetsa mtima wako kukuzindikira;
3
ukaitananso luntha, ndi kufuulira kuti ukazindikire;
4
ukaifunafuna ngati siliva, ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;
5
pompo udzazindikira kuopa Yehova ndi kumdziwadi Mulungu.
6
Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.
7
Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;
8
kuti atchinjirize njira za chiweruzo, nadikire khwalala la opatulidwa ake.
9
Pamenepo udzazindikira chilungamo ndi chiweruzo, zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.
10
Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,
11
kulingalira kudzakudikira, kuzindikira kudzakutchinjiriza;
12
kukupulumutsa kunjira yoipa, kwa anthu onena zokhota;
13
akusiya mayendedwe olungama, akayende m'njira za mdima;
14
omwe asangalala pochita zoipa, nakondwera ndi zokhota zoipa;
15
amene apotoza njira zao, nakhotetsa mayendedwe ao.
16
Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere, kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake;
17
wosiya bwenzi la ubwana wake, naiwala chipangano cha Mulungu wake.
18
Nyumba yake itsikira kuimfa, ndi mayendedwe ake kwa akufa;
19
onse akunka kwa iye sabweranso, safika kunjira za moyo;
20
nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino, kuti usunge mayendedwe a olungama.
21
Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko, angwiro nadzatsalamo.
22
Koma oipa adzalikhidwa m'dziko, achiwembu adzazulidwamo.
← Chapter 1
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 3 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31