bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 17
Proverbs 17
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 16
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 18 →
1
Nyenyeswa youma, pokhala mtendere, iposa nyumba yodzala nyama yansembe, pali makangano.
2
Kapolo wochita mwanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, nadzagawana nao abale cholowa.
3
Siliva ali ndi mbiya yosungunulira, golide ali ndi ng'anjo; koma Yehova ayesa mitima.
4
Wochimwa amasamalira milomo yolakwa; wonama amvera lilime losakaza.
5
Wochitira chiphwete aumphawi atonza Mlengi; wokondwera ndi tsoka sadzapulumuka chilango.
6
Zidzukulu ndizo korona wa okalamba; ndipo ulemerero wa ana ndiwo atate ao.
7
Mlomo wangwiro suyenera chitsiru; ngakhale mlomo wonama suyenera kalonga ndi pang'ono ponse.
8
Wolandira chokometsera mlandu achiyesa ngale; paliponse popita iye achenjera.
9
Wobisa cholakwa afunitsa chikondano; koma wobwerezabwereza mau afetsa ubwenzi.
10
Chidzudzulo chilowa m'kati mwa wozindikira, kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.
11
Woipa amafuna kupanduka kokha; koma adzamtumizira mthenga wankhanza.
12
Kukomana ndi chitsiru m'kupusa kwake kuopsa koposa chilombo chochichotsera anake.
13
Wobwezera zabwino zoipa, zoipa sizidzamchokera kwao.
14
Chiyambi cha ndeu chifanana ndi kutsegulira madzi; tsono kupikisana kusanayambe tasiya makani.
15
Wokometsa mlandu wa wamphulupulu, ndi wotsutsa wolungama, onse awiriwa amnyansa Yehova.
16
Kodi bwanji mtengo wogulira nzeru uli m'dzanja la chitsiru, popeza wopusa alibe mtima?
17
Bwenzi limakonda nthawi zonse; ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.
18
Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina, napereka chikole pamaso pa mnzake.
19
Wokonda ndeu akonda kulakwa; ndipo wotalikitsa khomo lake afunafuna kuonongeka.
20
Wokhota mtima sadzapeza bwino; ndipo mwini lilime lokhota adzagwa m'zoipa.
21
Wobala chitsiru adzichititsa chisoni; ndipo atate wa wopusa sakondwa.
22
Mtima wosekerera uchiritsa bwino; koma mzimu wosweka uphwetsa mafupa.
23
Munthu woipa alandira chokometsera mlandu chotulutsa m'mfunga, kuti apatukitse mayendedwe a chiweruzo.
24
Nzeru ili pamaso pa wozindikira; koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.
25
Mwana wopusa achititsa atate wake chisoni, namvetsa zowawa amake wombala.
26
Kulipiritsa wolungama sikuli kwabwino, ngakhale kukwapula akulu chifukwa aongoka mtima.
27
Wopanda chikamwakamwa apambana kudziwa; ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.
28
Ngakhale chitsiru chikatonthola achiyesa chanzeru; posunama ali wochenjera.
← Chapter 16
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 18 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31