bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 16
Proverbs 16
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 15
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 17 →
1
Malongosoledwe a mtima nga munthu; koma mayankhidwe a lilime achokera kwa Yehova.
2
Njira zonse za munthu ziyera pamaso pake; koma Yehova ayesa mizimu.
3
Pereka zochita zako kwa Yehova, ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.
4
Zonse Yehova anazipanga zili ndi zifukwa zao; ngakhale amphulupulu kuti aone tsiku loipa.
5
Yense wonyada mtima anyansa Yehova; zoonadi sadzapulumuka chilango.
6
Mphulupulu iomboledwa ndi chifundo ndi ntheradi; apatuka pa zoipa poopa Yehova.
7
Njira za munthu zikakonda Yehova ayanjanitsana naye ngakhale adani ake.
8
Zapang'ono, pokhala chilungamo, ziposa phindu lalikulu lopanda chiweruzo.
9
Mtima wa munthu ulingalira njira yake; koma Yehova ayendetsa mapazi ake.
10
Mau a mlauli ali m'milomo ya mfumu; m'kamwa mwake simudzachita chetera poweruza.
11
Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova; ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.
12
Kuchita mphulupulu kunyansa mafumu; pakuti mpando wao wakhazikika ndi chilungamo.
13
Milomo yolungama ikondweretsa mafumu; wonena zoongoka amkonda.
14
Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa; wanzeru adzaukhulula.
15
M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo; kukoma mtima kwake kunga mtambo wa mvula ya masika.
16
Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golide, kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?
17
Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa; wosunga njira yake atchinjiriza moyo wake.
18
Kunyada kutsogolera kuonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa.
19
Kufatsa mtima ndi osauka kuposa kugawana zofunkha ndi onyada.
20
Wolabadira mau adzapeza bwino; ndipo wokhulupirira Yehova adala.
21
Wanzeru mtima adzatchedwa wochenjera; ndipo kukoma kwa milomo kuonjezera kuphunzira.
22
Nzeru ndi kasupe wa moyo kwa mwini wake; koma mwambo wa zitsiru ndi utsiru.
23
Mtima wa wanzeru uchenjeza m'kamwa mwake, nuphunzitsanso milomo yake.
24
Mau okoma ndiwo chisa cha uchi, otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.
25
Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka, koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.
26
Wantchito adzigwirira yekha ntchito; pakuti m'kamwa mwake mumfulumiza.
27
Munthu wopanda pake akonzeratu zoipa; ndipo m'milomo mwake muli moto wopsereza.
28
Munthu wokhota amautsa makani; kazitape afetsa ubwenzi.
29
Munthu wa chiwawa akopa mnzake, namuyendetsa m'njira yosakhala bwino.
30
Wotsinzina ndiye aganizira zokhota; wosunama afikitsa zoipa.
31
Imvi ndiyo korona wa ulemu, idzapezedwa m'njira ya chilungamo.
32
Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; wolamulira mtima wake naposa wolanda mudzi.
33
Maere aponyedwa pamfunga; koma ndiye Yehova alongosola zonse.
← Chapter 15
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 17 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31