bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 24
Proverbs 24
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 23
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 25 →
1
Usachitire nsanje anthu oipa, ngakhale kufuna kukhala nao;
2
pakuti mtima wao ulingalira za chionongeko; milomo yao ilankhula za mphulupulu.
3
Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa.
4
Kudziwa kudzaza zipinda zake ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.
5
Mwamuna wanzeru ngwamphamvu; munthu wodziwa ankabe nalimba.
6
Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo, ndi kupulumuka pochuluka aphungu.
7
Nzeru italikira chitsiru; satsegula pakamwa kubwalo.
8
Wolingalira zakuchita zoipa anthu adzamtcha wachiwembu.
9
Maganizo opusa ndiwo tchimo; wonyoza anyansa anthu.
10
Ukalefuka tsiku la tsoka mphamvu yako ichepa.
11
Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse; omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.
12
Ukanena, Taonani, sitinadziwa chimenechi; kodi woyesa mitima sachizindikira ichi? Ndi wosunga moyo wako kodi sachidziwa? Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa machitidwe ake?
13
Mwananga, idya uchi pakuti ngwabwino, ndi chisa chake chitsekemera m'kamwa mwako.
14
Potero udzadziwa kuti nzeru ili yotero m'moyo wako; ngati waipeza padzakhala mphotho, ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.
15
Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama; usapasule popuma iyepo.
16
Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso; koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.
17
Usakondwere pakugwa mdani wako; mtima wako usasekere pokhumudwa iye;
18
kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa, ndi kuleka kumkwiyira.
19
Usavutike mtima chifukwa cha ochita zoipa; ngakhale kuchitira nsanje amphulupulu.
20
Pakuti woipayo sadzalandira mphotho; nyali ya amphulupulu idzazima.
21
Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe, osadudukira anthu osinthasintha.
22
Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka; ndipo ndani adziwa chionongeko cha zaka zao?
23
Izinso zili za anzeru, poweruza chetera silili labwino.
24
Wonena kwa woipa, Wolungama iwe; magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira.
25
Omwe amdzudzula adzasekera, nadzadalitsika ndithu.
26
Wobwezera mau oongoka apsompsona milomo.
27
Longosola ntchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda; pambuyo pake ndi kumanga nyumba yako.
28
Usachitire mnzako umboni womtsutsa opanda chifukwa; kodi udzanyenga ndi milomo yako?
29
Usanene, Ndidzamchitira zomwezo anandichitira ine ndidzabwereza munthuyo monga mwa machitidwe ake.
30
Ndinapita pa munda wa waulesi, polima mphesa munthu wosowa nzeru.
31
Taonani, ponsepo panamera minga, ndi kuwirirapo khwisa; tchinga lake lamiyala ndi kupasuka.
32
Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira, ndinaona ndi kulandira mwambo.
33
Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, kungomanga manja pang'ono m'kugona,
34
ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa.
← Chapter 23
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 25 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31