bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 18
Proverbs 18
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 17
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 19 →
1
Wopanduka afunafuna chifuniro chake, nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.
2
Wopusa sakondwera ndi kuzindikira; koma kungovumbulutsa za m'mtima mwake.
3
Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza; manyazi natsagana ndi chitonzo.
4
Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya; kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.
5
Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankho sikuli kwabwino, ngakhale kuchitira chetera wolungama.
6
Milomo ya wopusa ifikitsa makangano; ndipo m'kamwa mwake muputa kukwapulidwa.
7
M'kamwa mwa wopusa mumuononga, milomo yake ikhala msampha wa moyo wake.
8
Mau akazitape akunga zakudya zolongosoka, zotsikira m'kati mwa mimba.
9
Wogwira ntchito mwaulesi ndiye mbale wake wa wosakaza.
10
Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba; wolungama athamangiramo napulumuka.
11
Chuma cha wolemera ndicho mudzi wake wolimba; alingalira kuti ndicho khoma lalitali.
12
Mtima wa munthu unyada asanaonongeke; koma chifatso chitsogolera ulemu.
13
Wobwezera mau asanamvetse apusa, nadzichititsa manyazi.
14
Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala; koma ndani angatukule mtima wosweka?
15
Mtima wa wozindikira umaphunzira; khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.
16
Mtulo wa munthu umtsegulira njira, numfikitsa pamaso pa akulu.
17
Woyamba kudzinenera ayang'anika wolungama; koma mnzake afika namuululitsa zake zonse.
18
Maere aletsa makangano, nulekanitsa amphamvu.
19
Kupembedza mbale utamchimwira nkovuta, kulanda mudzi wolimba nkosavuta; makangano akunga mipiringidzo ya linga.
20
Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m'kamwa mwake; iye nadzakhuta phindu la milomo yake.
21
Lilime lili ndi mphamvu pa imfa ndi moyo; wolikonda adzadya zipatso zake.
22
Wopeza mkazi apeza chinthu chabwino; Yehova amkomera mtima.
23
Wosauka amadandaulira; koma wolemera ayankha mwaukali.
24
Woyanjana ndi ambiri angodziononga; koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.
← Chapter 17
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 19 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31