bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 29
Proverbs 29
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 28
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 30 →
1
Yemwe aumitsa khosi atadzudzulidwa kwambiri, adzasweka modzidzimuka, palibe chomchiritsa.
2
Pochuluka olungama anthu akondwa; koma polamulira woipa anthu ausa moyo.
3
Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wake; koma wotsagana ndi akazi adama amwaza chuma.
4
Mfumu akhazikitsa dziko ndi chiweruzo; koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.
5
Wosyasyalika mnzake atcherera mapazi ake ukonde.
6
M'kulakwa kwa woipa muli msampha; koma wolungama aimba, nakondwera.
7
Wolungama asamalira mlandu wa osauka; koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.
8
Anthu onyoza atentha mudzi; koma anzeru alezetsa mkwiyo.
9
Munthu wanzeru akatsutsana ndi munthu wopusa, ngakhale akwiya, ngakhale aseka, palibe mtendere.
10
Anthu ankhanza ada wangwiro; koma oongoka mtima asamalira moyo wake.
11
Chitsiru chivumbulutsa mkwiyo wake wonse; koma wanzeru auletsa nautontholetsa.
12
Mkulu akamvera chinyengo, atumiki ake onse ali oipa.
13
Waumphawi ndi wotsendereza akumana; Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.
14
Mfumu yolamulira osauka mwantheradi, mpando wake udzakhazikika kufikira nthawi zonse.
15
Nthyole ndi chidzudzulo zipatsa nzeru; koma mwana womlekerera achititsa amake manyazi.
16
Pochuluka oipa zolakwa zichuluka; koma olungama adzaona kugwa kwao.
17
Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa; nadzasangalatsa moyo wako.
18
Popanda chivumbulutso anthu amasauka; koma wosunga chilamulo adalitsika.
19
Kapolo sangalangizidwe ndi mau, pakuti azindikira koma osavomera.
20
Kodi uona munthu wansontho m'mau ake? Ngakhale chitsiru chidzachenjera, koma ameneyo ai.
21
Yemwe alera kapolo wake mwa ufulu kuyambira ubwana wake, pambuyo pake adzadziyesa mwana wobala.
22
Mwamuna wamkwiyo aputa makangano; waukali achuluka zolakwa.
23
Kudzikuza kwa munthu kudzamchepetsa; koma wokhala ndi mtima wodzichepetsa adzalemekezedwa.
24
Woyenda ndi mbala ada moyo wakewake; amva kulumbira, koma osawulula kanthu.
25
Kuopa anthu kutchera msampha; koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.
26
Ambiri afunafuna chiyanjano cha mkulu; koma chiweruzo cha munthu chichokera kwa Yehova.
27
Munthu woipa anyansa olungama; ndipo woongoka m'njira anyansa wochimwa.
← Chapter 28
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 30 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31