bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
/
Proverbs 13
Proverbs 13
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
← Chapter 12
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 14 →
1
Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate; koma wonyoza samvera chidzudzulo.
2
Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwake; koma moyo wa achiwembu udzadya chiwawa.
3
Wogwira pakamwa pake asunga moyo wake; koma woyasamula milomo yake adzaonongeka.
4
Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu; koma moyo wa akhama udzalemera.
5
Wolungama ada mau onama; koma woipa anyansa, nadzichititsa manyazi.
6
Chilungamo chitchinjiriza woongoka m'njira; koma udyo ugwetsa wochimwa.
7
Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu; alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi chuma chambiri.
8
Chiombolo cha moyo wa munthu ndicho chuma chake; koma wosauka samva chidzudzulo.
9
Kuunika kwa olungama kukondwa; koma nyali ya oipa idzazima.
10
Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.
11
Chuma cholandiridwa mokangaza chidzachepa; koma wokundika ndi dzanja adzaona zochuluka.
12
Chiyembekezo chozengereza chidwalitsa mtima; koma pakufika chifunirocho ndicho mtengo wa moyo.
13
Wonyoza mau adziononga yekha; koma woopa malangizo adzalandira mphotho.
14
Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo, apatutsa kumisampha ya imfa.
15
Nzeru yabwino ipatsa chisomo; koma njira ya achiwembu ili makolokoto.
16
Yense wochenjera amachita mwanzeru; koma wopusa aonetsa utsiru.
17
Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa; koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.
18
Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa; koma wolabadira chidzudzulo adzalemekezedwa.
19
Chifuniro chikondweretsa moyo chitachitidwa; koma kusiya zoipa kunyansa opusa.
20
Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.
21
Zoipa zilondola ochimwa; koma olungama adzalandira mphotho yabwino.
22
Wabwino asiyira zidzukulu zake cholowa chabwino; koma wochimwa angosungira wolungama chuma chake.
23
M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri; koma zinazo zimaonongeka posowa chiweruzo.
24
Wolekerera mwanake osammenya amuda; koma womkonda amyambize kumlanga.
25
Wolungama adya nakhutitsa moyo wake; koma mimba ya oipa idzasowa.
← Chapter 12
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 14 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31