bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Isaiah 1
Isaiah 1
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 53
Chapter 54
Chapter 55
Chapter 56
Chapter 57
Chapter 58
Chapter 59
Chapter 60
Chapter 61
Chapter 62
Chapter 63
Chapter 64
Chapter 65
Chapter 66
Chapter 2 →
1
Buku lino likufotokoza zinthu zimene Mulungu adaululira Yesaya, mwana wa Amozi, zokhudza Yuda ndi Yerusalemu pa masiku a Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda.
2
Chauta adati, “Tamvera, iwe mlengalenga, tchera khutu, iwe dziko lapansi, Ine Chauta ndikulankhula. Ndidabereka ana ndi kuŵalera, koma andigalukira.
3
Ng'ombe imadziŵa mwini wake, bulu amadziŵa kumene mwini wake amamdyetsera, koma Aisraele sadziŵa, anthu anga samvetsa konse.”
4
Ha, mtundu wochimwa, inu anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoipa, ana omira m'zoipa! Mudasiya Chauta, mudanyoza Woyera uja wa Israele, mudamufulatira kwathunthu.
5
Kodi ndi pati ndingakumenyeninso, popeza kuti mukupandukirapandukira? Aliyense mutu wake uli ndi mabala kale, ndipo mtima wake wafookeratu.
6
Kuchokera kuphazi mpaka kumutu palibe pabwino, ponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu. Mabala ake ngosatsuka, ngosamanga, ndiponso ngosapaka mafuta ofeŵetsa.
7
Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu aitentha. Alendo akukuwonongerani dziko inu muli pomwepo. Lasanduka bwinja, lagonjetsedwa ndi alendo.
8
Mzinda wa Yerusalemu watsala wokhawokha ngati nsanja m'munda wamphesa, ngati dinda m'munda wa minkhaka, ngatinso mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9
Chauta Wamphamvuzonse akadapanda kutipulumutsirako ena oŵerengeka, tikadaonongeka kotheratu ngati anthu a ku Sodomu ndi Gomora.
10
Tsono imvani zimene Chauta akukuuzani, inu akulu a ku Sodomu. Mvetsetsani zimene Mulungu wathu akukuphunzitsani, inu anthu a ku Gomora.
11
Chauta akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka? Zandikola nsembe zopsereza za nkhosa zamphongo ndi za mafuta a nyama zonenepa. Sindikuŵafunanso magazi a ng'ombe zamphongo ndi a anaankhosa ndi a atonde.
12
“Ndani amakulamulani kuti mubwere nazo zimenezi pamaso panga? Ndani amakuuzani kuti muzipondaponda m'mabwalo a Nyumba yanga?
13
Musabwere nazonso nsembe zanu zachabechabe. Utsi wake umandinyansa. Sindingapirire misonkhano yanu yamapemphero, kapenanso zikondwerero za pokhala mwezi ndi za Sabata, sindingapirire mapemphero oipitsidwa ndi machimo.
14
Zikondwerero zanu za pokhala mwezi ndi masiku anu oyera ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera, ndatopa nako kuŵapirira.
15
Mukamatambasula manja anu popemphera, sindidzayang'anako. Ngakhale muchulukitse mapemphero anu chotani, sindidzasamalako, chifukwa manja anu ndi odzaza ndi magazi.
16
Sambani, dziyeretseni, chotsani pamaso panga ntchito zanu zoipa. Inde, lekani kuchita zoipa.
17
Phunzirani kuchita zabwino. Funafunani chilungamo, opsinjidwa muŵathandize. Tetezani ana amasiye, muŵaimirire pa milandu yao akazi amasiye.”
18
Chauta akunena kuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu: chifukwa cha machimo anu mwafiira kwambiri, koma Ine ndidzakutsukani, inu nkukhala oyera kuti mbee. Mwachita kuti psuu ngati magazi, koma mudzakhala oyera ngati thonje.
19
Ngati muli okonzeka kundimvera, mudzalidyera dziko.
20
Koma mukakana ndi kumapanduka, mudzaphedwa ndi lupanga. Ine Chauta ndatero.”
21
Taonanitu! Mzinda umene kale udaali wokhulupirika ndi wachilungamo, tsopano ukuchita zadama. Mzinda umene kale udaali ndi anthu aungwiro, tsopano wadzaza ndi anthu opha anzao.
22
Iwe Yerusalemu, unali ngati siliva, koma tsopano wasanduka wopandapake. Unali ngati vinyo wabwino, koma tsopano uli ngati vinyo wosakanizika ndi madzi.
23
Atsogoleri ako apanduka, ndipo amagwirizana ndi mbala. Aliyense amakonda chiphuphu, ndipo amathamangira mphatso. Satchinjiriza ana amasiye, ndipo samvera madandaulo a akazi amasiye.
24
Nchifukwa chake Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse, Wamphamvu uja wa Israele, akunena kuti: “Ha! Olimbana nane ndidzaŵatha, adani anga ndidzaŵalipsira.
25
Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe. Ndidzasungunula machimo ako nkuŵachotsa, monga m'mene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26
Aweruzi ako ndidzaŵakhazikitsanso ngati pa masiku akale aja. Aphungu akonso ndidzaŵakhazikitsanso ngati poyamba paja. Pambuyo pake iweyo udzatchedwa mzinda waungwiro, mzinda wokhulupirika.”
27
Chauta ndi wolungama, adzaombola Ziyoni. Chauta ndi waungwiro, adzaombolanso anthu olapa amumzindamo.
28
Koma opanduka ndi ochimwa adzaŵaonongera pamodzi, osiya Chauta adzatheratu.
29
Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani, mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene mudaipatula.
30
Pakuti mudzafanafana ndi mtengo wa thundu wofota masamba, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31
Anthu amphamvu adzasanduka ngati udzu wouma, ntchito zao ngati mbaliŵali. Motero anthuwo adzayakira limodzi ndi ntchito zaozo, popanda woti auzimitse motowo.
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 53
Chapter 54
Chapter 55
Chapter 56
Chapter 57
Chapter 58
Chapter 59
Chapter 60
Chapter 61
Chapter 62
Chapter 63
Chapter 64
Chapter 65
Chapter 66
Chapter 2 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31
32
33
34
35
36
37
38
39
40
41
42
43
44
45
46
47
48
49
50
51
52
53
54
55
56
57
58
59
60
61
62
63
64
65
66
Recommended Reading
Commentary
Isaiah Commentaries
→
Devotional
Isaiah Devotional Guide
→
Get This Bible
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa) Study Bible
→