bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Isaiah 45
Isaiah 45
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 44
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 53
Chapter 54
Chapter 55
Chapter 56
Chapter 57
Chapter 58
Chapter 59
Chapter 60
Chapter 61
Chapter 62
Chapter 63
Chapter 64
Chapter 65
Chapter 66
Chapter 46 →
1
Chauta akulankhula ndi wodzozedwa wake Kirusi amene adamgwira dzanja lamanja, kuti agonjetse mitundu ina ya anthu, aŵathe mphamvu mafumu, ndi kutsekula zitseko kuti zipata zisatsekeke.
2
Akunena kuti, “Ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza zitunda. Ndidzaphwanyaphwanya zitseko zamkuŵa, ndipo ndidzathyolathyola mipiringidzo yake yachitsulo.
3
Ndidzakupatsa chuma chosaoneka poyera ndi katundu wa m'malo obisika. Motero udzadziŵa kuti ndine Chauta, Mulungu wa Israele, amene ndikukuitana pokutchula dzina.
4
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobe, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israele, ndikukuitana potchula dzina lako, ndikukupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziŵa.
5
Chauta ndine, palibenso wina, kupatula ine palibe Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu ngakhale sukundidziŵa.
6
Ndidzachita zimenezi kuti kuchokera kuvuma mpaka kuzambwe aliyense adziŵe kuti palibe wina koma Ine ndekha. Chauta ndine, palibenso wina.
7
“Ndimalenga kuŵala ndi mdima, ndimadzetsa madalitso ndi tsoka. Ndine, Chauta, amene ndimachita zonsezi.
8
“Gwetsa mvula, iwe thambo, kuchokera kumwamba, mitambo ikhuthule chilungamo chopulumutsa. Dziko lapansi litsekuke kuti patuluke chipulumutso, kuti chilungamo chimerepo. Ndine, Chauta, amene ndidalenga zimenezi.”
9
Tsoka kwa amene amakangana ndi mlengi wake, ngakhale ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi mtapo ungafunse munthu woumba kuti, “Kodi ukuumba chiyani?” Kapena kunena kuti, “Woumbawe, ulibe luso!”
10
Tsoka kwa wofunsa bambo wake kuti, “Mwabereka chiyani,” kapena mai wake kuti, “Mwabala chiyani?”
11
Chauta, Woyera uja wa Israele ndiponso Mlengi wake, akunena kuti, “Kodi iwe ungandifunse za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12
Ndine amene ndidalenga dziko lapansi ndi kulenga munthu kuti akhalemo. Ndidayalika zakuthambo ndi manja anga, ndipo tsopano ndimalamulira gulu lonse lamumlengalenga.
13
Ndine amene ndidautsa Kirusi kuti chilungamo chichitike. Ndidzaongola mseu uliwonse umene adzadzeramo. Adzamanganso mzinda wanga wa Yerusalemu ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, osapereka ndalama kapena mphotho,” watero Chauta Mphambe.
14
Chauta akuuza Aisraele kuti, “Chuma cha ku Ejipito ndi malonda a ku Etiopiya zidzakhala zanu. Anthu a ku Saba, a msinkhu aatali, adzabwera kwa inu ndi kukhala akapolo anu ndipo azidzakutsatani. Adzabwera ali omangidwa ndi maunyolo, ndi kukugwadirani. Adzakupembani ndi kunena kuti, ‘Mulungu ali ndi inu nokha, palibenso wina ai. Kupatula Iyeyo palibe mulungu wina.
15
Ndithu inu muli ndi Mulungu wobisika, amene ali Mulungu wa Israele ndiponso Mpulumutsi.
16
Onse amene amapanga mafano, adzaŵachititsa manyazi ndi kunyozetsa, adzamwazikana atasokonezeka.
17
Koma Israele amampulumutsa ndi Chauta, ndipo chipulumutso chake chidzakhalapo mpaka muyaya, Anthu ake sadzaŵachititsa manyazi konse, sadzakhala onyozeka konse.’ ”
18
Akutero Chauta amene adalenga zakumwamba, ndi Iyeyo Mulungu amene adaumba ndi kulenga dziko lapansi, ndipo adalikhazikitsa mwamphamvu. Sadalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma kuti likhale malo okhalamo anthu. Iyeyo akunena kuti: “Chauta ndine, palibenso wina ai.
19
Sindidalankhule mwachinsinsi pa malo ena m'dziko lamdima. Sindidauze zidzukulu za Yakobe kuti zizindifunafuna kumene kuli kopanda kanthu. Ine Chauta ndimalankhula zoona, ndimanena zolungama.”
20
Chauta akuti, “Musonkhane pamodzi ndipo mubwere. Musendere pafupi, inu nonse amene mudapulumuka kwa anthu a mitundu ina! Ndi opanda nzeru amene amanyamula mafano amitengo, namapemphera kwa milungu imene singathe kuŵapulumutsa.
21
Kambani, fotokozani mlandu wanu. Mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani adaneneratu zimene zidzachitika? Ndani adaloseratu kalekale zimenezo? Kodi si Ineyo, Chautane? Ndithu, kupatula Ine palibe Mulungu wina, Mulungu wachilungamo ndi wopulumutsa. Palibenso wina aliyense kupatula Ine.”
22
“Inu anthu onse a pa dziko lapansi, tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke. Paja Ine ndine Mulungu, palibenso wina ai.
23
Ndalumbira dzina langa lomwe, pakamwa panga palankhula moona mau amene sadzasinthika konse, akuti, ‘Bondo lililonse lidzandigwadira, anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.’
24
“Pokamba za Ine adzanena kuti, ‘Chilungamo ndiponso mphamvu zimapezeka mwa Chauta yekha. Onse amene ankamugalukira adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25
Koma mwa Chautayo zidzukulu zonse za Israele zidzapambana ndi kupeza ulemerero.’ ”
← Chapter 44
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 53
Chapter 54
Chapter 55
Chapter 56
Chapter 57
Chapter 58
Chapter 59
Chapter 60
Chapter 61
Chapter 62
Chapter 63
Chapter 64
Chapter 65
Chapter 66
Chapter 46 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31
32
33
34
35
36
37
38
39
40
41
42
43
44
45
46
47
48
49
50
51
52
53
54
55
56
57
58
59
60
61
62
63
64
65
66
Recommended Reading
Commentary
Isaiah Commentaries
→
Devotional
Isaiah Devotional Guide
→
Get This Bible
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa) Study Bible
→