bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Jeremiah 10
Jeremiah 10
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 9
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 11 →
1
Inu Aisraele, imvani mau amene Chauta akukuuzani,
2
Chauta akuti, “Musatsate makhalidwe a anthu a mitundu ina. Musachite mantha ndi zizindikiro zozizwitsa zamumlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha zimenezi.
3
Ndithudi, miyambo ya anthu a mitundu inayo nzopanda pake. Iwo aja amakadula mtengo ku nkhalango, munthu waluso namausema ndi nsompho.
4
Anthu ena amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide, kenaka nkuchikhomerera ndi misomali, kuti chisagwedezeke.
5
Mafano aowo ali ngati kangamunthu woopsera mbalame m'munda wa minkhaka, sangathe nkulankhula komwe. Ayenera kuŵanyamula, poti sangayende okha. Musaŵaope, chifukwa sangakuchiteni choipa. Alibenso mphamvu zochitira zabwino.”
6
Palibe wolingana nanu, Inu Chauta. Inu ndinu aakulu, dzina lanu lili ndi mphamvu yaikulu.
7
Ndani amene angaleke kukuwopani, Inu mfumu ya mitundu ya anthu? Paja kukuwopaniko nkokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse ndiponso pakati pa maufumu onse a pansi pano palibe wina wolingana nanu.
8
Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru. Nzeru zao amaphunzira ku mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
9
Siliva wosula wokutira mafanowo ndi wochokera ku Tarisisi, ndipo golide wake ndi wochokera ku Ufazi. Mafano aowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi anthu odziŵa kuzokota golide. Amaveka mafanowo nsalu zonyezimira ndi zofiirira. Zonsezo ndi ntchito ya anthu aluso chabe.
10
Koma Chauta ndiye Mulungu woona, Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo ndiponso Mfumu yamuyaya. Dziko lapansi limagwedezeka ndi ukali wa Chauta. Anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
11
Anthuwo mukaŵauze kuti, “Milungu imene sidalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzaonongeka ponseponse, pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.”
12
Chauta ndiye amene adalenga dziko lapansi ndi mphamvu zake. Ndiye amene adapanga zonse ndi nzeru zake ndipo ndi umisiri wake adayala thambo lakumwamba.
13
Iye akalankhula, kumamveka mkokomo wa madzi kumwamba, ndiye amene amadzetsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amang'animitsa mphezi za mvula, amakunthitsa mphepo kuchokera kumene amaisunga.
14
Anthu onse ndi opusa, alibe nzeru. Mmisiri aliyense wosula amachita manyazi ndi mafano ake. Mafano amene amapangawo ngabodza mwa iwo mulibe konse moyo.
15
Mafanowo ngachabechabe, ayenera kuŵaseka, ndipo pamene anthuwo adzalangidwe, mafanowo adzaonongeka.
16
Koma Iye uja amene ali choloŵa cha Yakobe sali ngati mafanowo, Iye ndiyedi Mlengi wa zonse. Aisraele ndi anthu ake amene Iye adaŵasankha, dzina lake ndi Chauta Wamphamvuzonse.
17
Tolatolani katundu wanu, osamsiyanso pansi, inu amene adani akuzingani ndi zithando zankhondo.
18
Chauta akunena kuti, “Tsopano ndichotsa anthu onse a m'dziko lino. Ndidzaŵagwetsa m'mavuto, mpaka aŵamve ndithu.”
19
Ali apa amvekere, “Kalanga ine chifukwa cha kupweteka koopsa! Bala langa ndi lomvetsa chisoni. Kale ndinkati chimenechi ndi chilango changa, ndingochipirira basi.”
20
Hema langa laonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso wina woti nkundikhomera hema, kapena woti nkufunyulula nsalu zake.
21
Paja abusa ndi opusa, sapempha nzeru kwa Chauta. Nchifukwa chake zinthu sizidaŵayendere bwino, ndipo nkhosa zao zidabalalika.
22
Tamvani, kukubwera mphekesera. Kumpoto kukuchokera chinamtindi chosokosa chodzasakaza mizinda ya Yuda, kuti isanduke bwinja, mokhala nkhandwe basi.
23
Inu Chauta, ndikudziŵa kuti moyo umene ali nawo munthu si wake. Munthu sangathe kudzitsogolera yekha.
24
Langizeni, Inu Chauta, koma mwachilungamo. Musandikwiyire kuti mungandiwononge.
25
Ukali wanu uyakire mitundu imene sikudziŵani, ndiye kuti anthu amene satama dzina lanu mopemba. Iwo adasakaza anthu anu ndi kuŵaononga kotheratu ndipo dziko lao adalisandutsa bwinja.
← Chapter 9
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 11 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31
32
33
34
35
36
37
38
39
40
41
42
43
44
45
46
47
48
49
50
51
52