bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Jeremiah 43
Jeremiah 43
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 42
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 44 →
1
Yeremiya atatsiriza kuuza anthu zonse zimene Chauta Mulungu wao adamtuma kuti akaŵauze,
2
Azariya mwana wa Hesaya, Yohanani mwana wa Kareya, ndiponso anthu onse achipongwe, adauza Yeremiya kuti, “Iwe ukunama. Chauta Mulungu wathu sadakutume kudzanena kuti, ‘Musapite ku Ejipito kukakhala kumeneko.’
3
Baruki mwana wa Neriya ndiye wakukakamiza kuti utiletse, ndipo kuti tigwe m'manja mwa Ababiloni, kuti atiphe kapena kutitenga ukapolo kupita ku Babiloni.”
4
Tsono Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo, pamodzi ndi anthu onse a ku Yuda, adakana kumvera Chauta ndipo sadakhale ku Yuda.
5
Choncho Yohanani mwana wa Kareya, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo, adatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene adabwerera kuchokera ku maiko kumene adaabalalikira kuti akakhale ku Yuda.
6
Anthuwo anali aŵa: amuna, akazi ndi ana, kuphatikizapo ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu onse amene Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo adaaŵasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani. Adatenganso mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
7
Onsewo adapita nawo ku Ejipito monyoza mau a Chauta, nakafika ku Tapanesi.
8
Chauta adalankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi. Adamuuza kuti,
9
“Tenga miyala ina yaikulu, uikwirire m'dothi pa chiwundo cha poloŵera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Ayuda akuwone ukuchita zimenezo.
10
Tsono uŵauze kuti Chauta Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israele, akunena kuti, ‘Ndidzaitana mtumiki wanga Nebukadinezara, mfumu ya ku Babiloni. Iyeyo adzaika mpando wake pa miyala imene ndaibisa apoyo. Ndipo adzafunyulula hema lake laufumu pa miyalayo.
11
Adzabwera kudzaononga Ejipito, adzatumiza mliri pa anthu oyenera kufa ndi mliri, adzatenga ukapolo anthu oyenera kutengedwa ukapolo, ndipo adzaŵapha ndi lupanga oyenera kuphedwa ndi lupanga.
12
Adzasonkha moto m'nyumba za milungu ya ku Ejipito. Adzatentha nyumbazo, ndipo milunguyo adzaitenga kupita nayo ku ukapolo. Adzayeretsa dziko la Ejipito monga momwe mbusa amamangira chovala chake m'chiuno, momwemonso ndimo adzaŵachitire Aejiptio ndipo adzachoka ku Ejipito osaona vuto lililonse.
13
Adzaphwanya zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzeramo mulungu wa dzuŵa ku Ejipito. Ndipo adzatentha nyumba za milungu ya ku Ejipito.’ ”
← Chapter 42
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 44 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31
32
33
34
35
36
37
38
39
40
41
42
43
44
45
46
47
48
49
50
51
52