bible
ra
🌐 Language
English
Español
Français
Deutsch
Português
Italiano
Nederlands
Русский
中文
日本語
한국어
العربية
Türkçe
Tiếng Việt
ไทย
Indonesia
All Languages
Home
/
Chewa
/
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
/
Jeremiah 3
Jeremiah 3
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
← Chapter 2
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 4 →
1
Chauta akuti, “Munthu akasudzula mkazi wake, mkaziyo nkuchoka, nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumtenganso mkaziyo? Kodi atachita zotero, sindiye kuti dzikolo laipitsidwa kwambiri? Tsono iwe Israele, wachita zadama ndi abwenzi ambiri. Kodi ungabwererenso kwa Ine?
2
Uyang'ane ku zitunda zonse zachipembedzo. Mpoti pamene sudachitepo zadama? Unkakhala m'mbali mwa njira kumadikirira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu m'chipululu. Waipitsa dziko ndi mkhalidwe wako woipa wachiwerewere.
3
Nchifukwa chake Chauta adaimitsa mvula, ndi mvula yam'masika yomwe sidagwe. Komabe maonekedwe ako onse nga mkazi wachiwerewere, ndipo ulibe ndi manyazi omwe.
4
Kodi si tsopano apa wakhala ukundiwuza kuti, ‘Atate, ndinu bwenzi la unyamata wanga,’ numadzifunsa kuti,
5
‘Kodi Chauta adzandipsera mtima nthaŵi zonse? Kodi adzakwiya mpaka muyaya?’ Umu ndimo m'mene unkalankhulira. Komabe iwe udapitiriza kuchita zoipa monga momwe unkathera.”
6
Pa nthaŵi ya mfumu Yosiya, Chauta adati, “Kodi waona zimene wosakhulupirika uja Israele adachita? Ankakwera kukapembedza pa phiri, ndi patsinde pa mtengo uliwonse wogudira. Motero kumeneko ankakachita zadama.
7
Ndidaaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sadabwerere. Tsono Yuda, mbale wake wosakhulupirika uja, adaziwona zimenezo.
8
Adaona kuti Israele wosakhulupirika uja ndidamsudzula ndi kumpirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda, mbale wake, sadaope. Iyenso adakhala wosakhulupirika, adapita kukachita zadama.
9
Dama la Israele linali lochititsa manyazi, kotero kuti potsiriza pake adaipitsa dziko. Adachita chigololo popembedza mafano amiyala ndi amitengo.
10
Komabe atachita zonsezi, Yuda mbale wake wosakhulupirika uja sadabwerere kwa Ine ndi mtima wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akuterotu Chauta.
11
Chauta adandiwuzanso kuti, “Israele wosakhulupirika uja kupalamula kwake nkochepa, kuyerekeza ndi Yuda wosakhulupirika uja.
12
Pita ukalalike kumpoto uthenga uwu wakuti, “ ‘Israele wosakhulupirikawe, bwerera,’ akuterotu Chauta. ‘Ukali wanga sudzapitirira, poti ndine wachifundo. Sindidzakukwiyira mpaka muyaya.
13
Ungovomera kulakwa kwako. Vomera kuti udaukira Chauta Mulungu wako, kuti udapembedza nao milungu yachilendo patsinde pa mitengo yogudira, ndiponso kuti sudamvere mau anga,’ ” akuterotu Chauta.
14
“Bwererani inu anthu osakhulupirika, pakuti mbuye wanu ndine. Ndidzakutengani kupita nanu ku Ziyoni, mmodzi kuchokera ku mzinda uliwonse, aŵiri kuchokera ku banja lililonse.
15
“Kumeneko ndidzakupatsani abusa a kukhosi kwanga. Adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
16
Masiku amenewo mukadzachulukana m'dzikomo, anthu sadzalankhulanso za bokosi lachipangano la Chauta. Sadzaliganizira kapena kulikumbukira kapena kulisoŵa, ndipo sadzapanganso lina.
17
Nthaŵi imeneyo Yerusalemu adzatchulidwa Mpando waufumu wa Chauta. Ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana kumeneko pamaso pa Chauta. Sadzaumiriranso kutsata mtima wao woipa.
18
Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphathana ndi fuko la Israele. Onse pamodzi adzachokera ku dziko lakumpoto kupita ku dziko limene ndidapatsa makolo ao, kuti likhale choloŵa.”
19
Chauta akunena kuti, “Iwe Israele, ndikadakonda kukukhazika pakati pa ana anga, ndi kukupatsa dziko lokoma, choloŵa chokongola kwambiri kupambana maiko a mitundu ina ya anthu. Ndidaganiza kuti udzanditchula ‘Atate’, ndipo kuti sudzaleka kumanditsata.
20
Ndithu, monga momwe mkazi wosakhulupirika amasiyira mwamuna wake, iwenso Israele wakhala wosakhulupirika kwa Ine,” akuterotu Chauta.
21
Pakumveka liwu pa magomo, Aisraele akulira ndiponso akupempha chifundo, pakuti atsata njira zoipa, ndipo aiŵala Chauta, Mulungu wao.
22
“Bwererani kwa Ine, inu anthu anga osakhulupirika. Ndidzakuchiritsani kuti mukhale okhulupirika.” Inu mukuti, “Tikubwera kwa Inu, poti ndinu Chauta, Mulungu wathu.
23
Kupembedza pa magomo sikuthandiza, kuchita maphwando pa mapiri kulibenso ntchito. Zoonadi, mwa Chauta, Mulungu wathu ndiye muli chipulumutso cha Israele.
24
“Kuchokera pa chiyambi cha mtundu wathu, Baala, mulungu wochititsa manyazi uja, wakhala akutiwonongetsa phindu la ntchito ya makolo athu, ndiye kuti nkhosa ndi ng'ombe zao, ana ao aamuna ndi ana ao aakazi.
25
Tsono tigone pansi mwamanyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tidachimwa ife pamodzi ndi makolo athu, kuchimwira Chauta Mulungu wathu, kuyambira ubwana wathu mpaka lero lino. Sitidamvere mau a Chauta Mulungu wathu.”
← Chapter 2
Jump to:
Chapter 1
Chapter 2
Chapter 3
Chapter 4
Chapter 5
Chapter 6
Chapter 7
Chapter 8
Chapter 9
Chapter 10
Chapter 11
Chapter 12
Chapter 13
Chapter 14
Chapter 15
Chapter 16
Chapter 17
Chapter 18
Chapter 19
Chapter 20
Chapter 21
Chapter 22
Chapter 23
Chapter 24
Chapter 25
Chapter 26
Chapter 27
Chapter 28
Chapter 29
Chapter 30
Chapter 31
Chapter 32
Chapter 33
Chapter 34
Chapter 35
Chapter 36
Chapter 37
Chapter 38
Chapter 39
Chapter 40
Chapter 41
Chapter 42
Chapter 43
Chapter 44
Chapter 45
Chapter 46
Chapter 47
Chapter 48
Chapter 49
Chapter 50
Chapter 51
Chapter 52
Chapter 4 →
All chapters:
1
2
3
4
5
6
7
8
9
10
11
12
13
14
15
16
17
18
19
20
21
22
23
24
25
26
27
28
29
30
31
32
33
34
35
36
37
38
39
40
41
42
43
44
45
46
47
48
49
50
51
52